Chichewa Malankhulidwe ena
Tsiku ndi tsiku mungathe kugonjetsa zoipa mwa mphamvu ya Mzimu Woyera.  Kwa Mkristu amene adziwa ndi kudzazidwa ndi Mzimu Woyera.

Kodi Munapeza Moyo wa Uzimu?

 

M'buku la Mau a Mulungu tiwerenga za anthu a mitundu itatu:

1.  Munthu Amene Sanamulandile Yesu Kristu M'moyo Wace.
  "Munthu amene alibe Mzimu Woyera, amakana zimene zili za Mzimu wa Mulungu.  Amaziyesa zopusa, ndipo sngathe kudziwa, popeza kuti munthu amazindikira pokhapokha atakhala ndi Mzimu Woyera" (1 Akorinto 2:14).

MUNTHU AMENE SALI MKRISTU.

INE ndiri pa mpando.  Munthu mwini wake amalamulira zonse za moyo wake.

Zamoyo zace zonse zasokonezeka. 

YESU ali pabwalo, salandiridwa.


2.  Mkristu wodzala ndi Mzimu Woyera.
"Koma chipatsi cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro, chifatso, chiletso, pokana zimenezi palibe lamulo (Agalatiya 5;22'23).

law4.2.gif (4586 bytes) MKRISTU ODZALA NDI MZIMU OYERA

YESU ndiye mfumu ndipo alamulira za m'moyo wange.

INE ndibvomela ndi kutumikira Yesu.

Zamoyo zanga zonse zalongosoka.

 


3.  Mkristu Wodzilamulira yekha.
  "Ndipo ine abale, sidinakhoza kulankhula ndi inu monga ndi auzimu, koma monga athupi, monga makanda mwa Kristu.  Ndnadyetsa inu mkaka, sichakudya cholimba ayi; pakuti simunachikhoza; pakuti mulino athupi; pakuti pokhala pali nkhwidzi ndi ndeu pakati pa inu, simuli a thupi kodi?  Ndikuyendayenda monga mwa munthu?"
(1 Akorinto 3:1-3).

law4.5.gif (4425 bytes) MKRISTU WODZILAMULIRA YEKHA

INE ndiri pa mpando

Yesu acotsedwa pa mpando.  Sasogolela moyo wanga.

Za moyo zanga zisokonezeka

 

1. Mulungu atipasta ife moyo ocuruka ndiponso wa zipatso mu Cikritu.
  • Yesu Akuti, "Ndaza kuti akhale ndi moyo, ndikukhala nao ocuriuka" (Yohane 10:10).

  •   "Ine ndine mpesa, inu ndinu nthambi zace: wakukukhala mwa ine, ndi ine mwa iye, ameneyo abala chipatso cambiri, pakuti popanda ine inu simungathe kucita kanthu" (Yohane 15:5).
  •   "Koma cipatso ca uzimu ndico cikondi, cimwemwe,mtendere, kuleza mtima, cifundo, kikoma mtima, cikhulupiriro, cifatso, ciletso: pokana zimenezi palibe lamulo" (Agalatiya 5:22, 23).
  •   "Komatu mudzalandira mphavu, Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo mudzakhala mboni zanga m'Yerusalemu, ndi m'Yudeya lonse, ndi m'Samariya, ndi kufikira malekezero ace a dziko"(Macitidwe 1:8).

    Mkristu wodzala ndi Mzimu Woyera 
Amalola Yesu kukhala pa mpando, ali ndi mphamvu yopatsidwa ndi Mzimu Woyera wokhala mwa iye. 
Amafitsa anthu ena kwa Yesu
Amapemphera mwa chikhulupiriro
law4.2.gif (4586 bytes) Chikondi
Chimwemwe
Mtendere
Kukoma-mtima
Kukhulupilira
Kuleza mtima
Cifatso
Ciletso


Ngati Mkristu akhala ozipereka kwa Mulungu Atate tsiku ndi tsiku muz adzakhala wakukula mucikristu chace. 

Kodi ndi cifukwa ciani anthu ambirir amasowa moyo weni-weni wabino?

2. Mkristu wodzilamulira Yekha.

Mkristu wodzilamulira amangofuna kudzikonweretsa yekha nthawi zonse, osati kukonweletsa Mulungu.

  1. Ameneyo saziwa kapena aiwala za chikondi ndi kukuhulukidwa ndi mpamvu za Ambuye Yesu.  (Aroma 5:8-10; Ahebri 11:2;  I John 1:1-3; 2 Petro 1:9; Macitidwe 1:8).
  2. Kawirikawiri amagonjera zoipa ndikulephera kukhala mkristu wa moyo woculuka.
  3. Mwina afunitsitsa kukondweretsa Mulungu koma amalephera.
  4. Salola Mzimu Oyera ku umupatse mphamvu.

(1 Akorinto 3:1-3; Aroma 7:15-24; 8:7; Agalatiya 5:16-18)


Mkristu wodzilamulira yekha- Chithunzi ichi chifanizira munthu wodzilamulira yekha:

Mkristuyu...
Sakhulupirira Mulungu ndi mtima wake onse
Amakhala osanvera Mulungu
Sadandaulila ena kuti alandire Yesu
Mtima wace sugundira kupemphera
law4.5.gif (4424 bytes) Maganizo Oipa
Nsanje
Nkhawa
Kuptsa mtima
Kuweruza ena
Kukhumudwa
Kuda nkhawa
Kufoka mtima
Kukhumudwa


(Munthu amene alankhula kuti ndi Mkristu koma  umoyo wace suonetsa zipatso za Uzimu, m'eneyo si Mkristu ayi . Tiyeni tione momwe tingathe kulandirila Yesu).

Coona Ca Citatu Citionetsa Njira...

3. Yesu alonjeza moyo ocuruka ndipo wa zipatso cifukwa co dzazidwa ndi Mzimu Woyera. 

Kusogoleledwa ndi Mzimu Woyera  ndi kustsogoleredwa ndi Yesu Kristu, ndipo Yesu atipatsa mphavu zogonjetsa zoipa(Yohane 15).

  • Ife tasandulika kuti tikhale akristu pokhulupilira Yesu Kristu kuti ndiye Mpulumutsi wathu.  Tisandulikanso akristu wodzala ndi Mzimu Woyera mwa kukhulupirira.  Ngakhale ali ndi Mzimu Woyera, sionse amene atsogoleledwa ndi Mzimu Woyera.

  • Mzimu Woyera utipatsa moyo ocuruka (Yohane7:37-39).

  • Mzimu Woyera unadza ku pereka ulemelelo kwa Yesu Kristu.  Pamene tidzazidwa ndi Mzimu Woyera, tikhala ophunzira eni-eni a Yesu Kristu.
  • Mu lamulo yakhe yosiliza pamene sanaunkhe kwa Atete ace, Yesu analonjeza Kutuma Mzimu Oyera kuti ife ticile umboni oona (Macitidwe1:1-9).

Kodi ndigalandile bwaji Mzimu Oyera?

4. Ife tasandulika kuti tikhale akristu pokhulupilira Yesu Kristu kuti ndiye Mpulumutsi wathu.  Tisandulikanso akristu wodzala ndi Mzimu Woyera mwa kukhulupirira. .

Mungathe kupempha tsopano kuti Mzimu Woyera adzaze ndi kulamulira moyo wanu:

  • Funitsitsani kutsogololedwa ndi Mzimu Oyera. (Mateyo 5:6; Yohane 7:37-39). 

  • Lapani machimo anu. Mwacikhulupiliro dziwani kuti Mulungu akhululikila macimo anu onse cifukwa Yesu Kristu anakufereni za kwaipa zanu zonse (Akolose 2:13-15; 1 Yohane 1; 2:1-3; Aheberi 10:1-17).

  • Dziperekeni kwathunthu kwa Mulungu (Aroma 12:1,2).

  • Khulupilirani kuti Mulungu adzachita:

    1. Ndi Lamulo -  Mulungu alamula kuti tidzazidwe, "Ndipo musaledzere nayo vinyo, m'mene muli chitayiko; koma mudzale naye Mzimu (Aefenso 5:18).

    2. Ndi Lonjezo - Mulungu alonjeza kuti adzatimvera. "Ndipo uku ndi kulimba mtima kumene tili nako kwa iye, kuti ngati tipempha kanthu monga mwa chifuniro chake, atinvera; ndipo ngati tidziwa kuti atinvera chilichonse tichipemph, tidziwa kutitilinazo izi tazipempha kwa iye." (1 Yohane 5:14, 15).

Mwacikulupiriro munkhathe kupemphera...

Mungathe Kudzazidwa ndi Mzimu Woyera Tsopano

Tilandila Mzimu Woyera pamene tipemphera mwacikulupiriro.  Pempherani ndipo khululupirani kuti mulndira Mzimu Woyera.

"Ambuye Yesu, ndivomera kuti ndakhala ndili kulamulira moyo wang ndeka.  Ndazindikira kuti mwakutero ndiri kuchimwira inu.  Tsopano ndaleka njira iyi.  Ndifuna kuti inu mulamulire myo wanga wonse.  motero ndidzipereka kwa inu.  Khalani mfumu mu mtima mwanga.  Khululukirani chimo langa, ndipo ndimupemphani kuti mudzaze moyo wanga ndi Mzimu wanu Woyera.  Zikomo Ambuye, ndikhulupirira kuti  munandikhululukira tchimo langa ndipo munandidzazadi ndi Mzimu Woyera, monga munalonjeza m Mawu anu."
Amen


M'mene mungadziwire kuti mwadzazidwa ndi Mzimu Woyera.

Mulungu alamulilra kuti tidzazidwa ndi Mzimu Woyera, ndipo alonjeza kuti adzatinvera tikapempha kalikonse kokomera Iye.  Munapempha chimene analamulira.  kodi mudziwa kuti mwalandira?.

 

Khulupirirani Mulungu, zina zibwera m,mbuyo
 Chitunzi ichi cha stima chitifanizira momwe ife tingathe kudzazidwa ndi Mzimu Woyera mwakukhulupirira malonjezo a Mulungu.


  1. Mutu wa sitima ufanizira mphavu ili ndi Mulungu ndi Mau ace.
  2. Mwachikhulupiriro tilumikizidwa ku mphavu, imeneyo.
  3. Zina zotsimikizira kuti tapulumutsidwa, zibwera pambuyo.

Umo mukhoza kukhalabe wodzala ndi Mzimu Woyera.

Mkristu angathe kukhala ndi moyo wodzala ndi Mzimu pokhapokha pamene iye akhulupilira Mulungu.
Pamene Mzimu Woyera atsogolera ndi kulamulira moyo wanu:

  1. Zipatso za Mzimu Woyera zidzachulukilabe m'moyo wanu (Agalatiya 5:22,23).
  2. Mapemphero anu adzakhala ndi mpamvu (Yakobo 5:16)
  3. Kudzindikira kwanu kwa Mua a Mulungu kudzaonjezeka tsiku ndi tsiku (2 Timoteo 3:16).
  4. Mudzalandira mphamvu yakuchitira Yesu umboni (Machitidwe 1:8)..
  5. Mudzakhala ndi mphamvu yogonjetsa nayo tchimo ndi mayesero a Satana (1 Akorinto 10:13)

Kupuma mu Uzimu

Mukachimwanso mwa kulanda mpando wachifumu kuti mulamulire moyo wanu, muyenera kuchita zinthu ziwiri izi:

  1. Lapani pa maso pa Mulungu pakuti mukachimwa mwa kuchita chifuniro chanu kusanvera Iye.  Mukatero Iye zdzakukhulukirani ndi kukuyeretsaninso (1 Yohane 1:9).

  2. Dziperekeni kwa Yesu Kristu kuti iye alamulire moyo wanu wonse (Aroma 6:13).
    Khulupilirani Mulungu kuti Iye adzakudzazaninso ndi Mzimu Woyera.  Kumbukirani pa Aefenso 5:18 Iye alamulila kuti mudzazidwe ndi Mzimu Woyera.  Ndipo pa 1 Yohane 5:14,15, alonjeza kuti Iye amatimvera tikapempha kanthu kalikonse komkomera Iye.  muchite zinthu izi ziwiri; kulapa ndi kulandira chikhululukiro pa nthawi iliyonse pamene Mzimu Woyera akusonyezani kuti munachimwa.  Mukatero mudzakhala ndi moyo weniweni wosefukira nthawi zonse (Yohane 10:10).

Zimene mwalandira, gawani kwa Munthu wina.

Anthu ambirir-mbiri akhala nalo danga yowerenga aka kabuku "Kodi munapeza Moyo weni-weni wa Uzimu".  Aka kabuku kapezeka mumalankhulidwe yosiyna-sina pa dziko lonse lapansi. Pamene Mkristu apeza moyo weni-weni wa mu Uzmui, panenepo akhala ndi mphamvu  mu moyo wace.  Ngati iye alola Mzimu Woyera kuti umulamulile agonjetsa chimo, apewa zoipa ndipo amvera Mau a Mulungu.

Ngati mufuna kugula zomwe mwawerenga, munghate kugula lelo.

Zofunika Zina

 Ngati Browser yanu sitha kuona mafomu aya tumani lamya kapena lembani kalata ku: 260-1-291272

Campus Crusade for Christ- Zambia
P.O. Box 36176
Lusaka, Zambia

Home Yesu Ndi Yani? Kanema ya YESU Malamulo Anai Moyo wa Uzimu Mwayi Chuma

© 2002 Campus Crusade for Christ International

Last Updated: 14 March, 2002